|  
               
               Stonecroft Stonecroft Training Mndandanda wa Utatu Malangizo Otsogolera Mavesi a m'BaibuloAdult Stonecroft International The International Team  English YDT Teachings Maphunziro a AnaMalawi Moringa Projects    |  | home >>stonecroft>> 
            yesu ndani?  >>phunziro 1          
            
             
            Stonecroft - YESU NDI NDANI?- Phunziro #1 
 
  
              Baibulo limati Chani za Yesu?
 
 
               
                | Yesu ndi 
                    Ndani?   Sauli, munthu wachiyuda amene amamanga ndi kupha akristu 
                    oyambirira, anafunsa funso lofunikira. Ndifunso lofunikira 
                    limene tingafunse. Anafunsa, "Ndinu ndani, Ambuye?" 
                   Analandira yankho pompopompo "Ndine Yesu amene ukumulondalonda..."
 (Machitidwe 9:5).
 Munthu waukaliyu (amene anapamgitsa chipolowe mu chalitchi 
                    choyambirira ku Yerusalem) analandira uthenga woyenera, anakhala 
                    munthu wosandulika. Anali atatakasidwa ndi chikhulupiriro 
                    chabodza. Ankaganiza kuti anali kukondweretsa Mulungu pochita 
                    ntchito zake zakupha, koma iye amkalondalonda Iye.  Timachita zomwezo, pamene tikukhulupirira zinthu zimene zili 
                    zabodza. Timachita zinthu zimene zili zoyipa kwa ife eni—nkhakhalenso 
                    kwa anzathu. Njira yokhayo kuti tikhale ndi chidziwitso chenicheni 
                    ndi kuzindikira ndi kukhulupirira choonadi. Maphunziro a Baibulowa 
                    akumana ndi chosowa chanu cha choonadi. Akukankhirani ku chitsime 
                    cha zoonadi zonse, Mau a Mulungu. Mulungu akuti, “Thambo ndi dziko lapansi 
                    zidzachoka, koma mau anga sadzachokaHeaven.”
 —Mateyu 24:35  Mau a Mulungu ndi oona ndipo adzaima mpaka kalekale. Anthu 
                    ali ndi zidziwitso zolakwika za Yesu.  |  People have many incorrect and strange ideas 
              about Jesus. Since our behavior is influenced and motivated by what 
              we believe, it is important that we have accurate information about 
              who Jesus is, who God is and who we are. When you have finished 
              this study, you will know beyond a shadow of a doubt who Jesus really 
              is. 
               
                | Mumakhulupirira kuti Yesu ndi ndani? 
                  Lero timamva maganizo osiyanasiyana. Ena amati ndiye amene anayambitsa 
                  chipembedzo....mtsogoleri wa nkulu wa chikristu...mphunzitsi 
                  wa nkulu wa chikhalidwe...munthu woyamba kuzunzidwa mwankhanza 
                  mum'bado wake. Titha kudziwa zoona pokhapoka tikakhulupirira uthenga wochokera 
                    ku chitsime cha choonadi. Pali choonadi chimodzi—Mulungu. 
                    Watipatsa ife Buku, limene limatiuza m'mene tingamudziwire 
                    Iye komanso m'mene tingakhalire moyo womusangalatsa Iye ndi 
                    ife. Yesu sali ngati m'modzi wa atsogoleri a chipembedzo pa dziko 
                    la pansi. Sali ngati munthu wankulu wa m'Baibulo ngati Abraham, 
                    Mose, kapena Davide. Nthawi zonse tikamalemba tsiku kapena 
                    chaka, timazindikira kuti zaka zikwi ziwiri (2000) zapitazo 
                    Yesu Khristu anabwera ndi kugawa mbiri m'magawo awiri:
 
 |  
               
                | Baibulo limatiuza zinthu zambiri zodabwitsa za 
                  Yesu. Mwachitsanzo, Yesu analipo chikhalire nthawi isanayambe. 
                  Malo ambiri mu Baibulo amafotokoza Yesu analipo pachiyambi dziko 
                  lisanalengedwe. Baibulo limati,  “Ndipo Iye ali woyamba wa sonse. 
                    . .”—Akolose 1:17
 
 |  
 
               
                | Yesu analipo asanabadwe ngati munthu. 
                  Wakhala ali chikhalire ndipo adzakhala mpaka muyaya. Palibe 
                  mtsogoleri wa chipembedzo amwene ananena kuti adzakhala muyaya, 
                  koma Yesu ananena. Anati, “ . . . Asanayambe 
                    kukhala Abraham ndipo 'Ine ndiripo'.”—Yohane 8:58
 Izi zitanthauza Yesu analipo. INE AMENE NDILI ndi dzina la 
                    Mulungu. Pa Exodo 3:14, zaka zikwi ziwiri Yesu asanabadwe, Mulungu 
                    anadzionetsera Yekha kwa Mose ngati "INE AMENE NDILI" 
                    Muchiheberi dzinali litanthauza kukhala kwa chikhalire. Yesu anaziyerekeza Yekha ndi Mulungu (Yohane 5:18)  |  Kuzindikira Choonadi 
               
                |  
                    Ganizani mozama ndi mwapemphero za maphunziro 
                      mukuphunzirawa.zifunseni mafunso awa:
 Baibulo pa gawo ili likuti chani?Zindikirani choona cha Mulungu
 Baibulo pa gawo ili likuti chani?Mvetsetsani chimene Mulungu akunena.
 Mulungu akundilankhula chani?Chitengeni choonacho muchichite pa moyo wanu.
 |  
               
                | Mwapempero 
                    lingalilani m'mene Mulungu akufunira kuti Muyankhe Muvera lamulo kapena kusintha 
                    m'mene mumaonera zinthu? |  
               
                | Uthenga 
                    wa Bwino   Mabuku oyambirira a Chipangano cha Tsopano sanalembedwe kukhala 
                    a mbiri ya Yesu. analembedwa ndi anthu osiyanasiyana kwa magulu 
                    osiyanasiyana ndi zifukwa zosiyanasiyana. mabuku amenewa amatchedwa 
                    uthenga wabwino. Awiri amabukuwa—Uthenga Wabwino wa Mateyu ndi Uthenga 
                    Wabwino wa Yohane—unalembedwa ndi anthu awiri amene 
                    anayenda ndi Yesu kwa zaka zitatu. anali mu gulu la anthu 
                    khumi ndi awiri amene Yesu adawasankha ngati atumwi. Pa mu 
                    chipangano cha Tsopano pali mndandanda wa mau amene akupereka 
                    tanthauzo la mau amene simukuwadziwitsitsa. Onani tanthauzo 
                    la mtumwi. . . . . Kuyambira pa ndi gawo losonyeza maphunziro. izi zimathandiza 
                    mukafuna kufufuza kuchoka mu Baibulo za phunziro limene mukufuna 
                    kuphunzira. Mateyu adalemba uthenga wa bwino wa Mateyu kutsimikizira 
                    a Yuda kuti iye ndiye Mesiya amene adakhala akumufunafuna. 
                   Yohane adalemba uthenga wabwino wa Yohane kutsimikizira owerenga 
                    kuti Yesu adali Mwana wa Mulungu.  Uthenga wa bwino wa Mariko udalembedwa ndi mnyamata Maliko, 
                    amene adagwira ntchito ndi Paulo komanso Barnaba ndi Petulo. 
                    Marko adalemba kwa amitundu kuwauza za Yesu ndi zimene 
                    adachita.  Uthenga wa bwino wa Luka udalembedwa ndi dotolo wa chihelena 
                    amene anapanga kafukufuku ndi ku fusa anthu amene anali kumudziwa 
                    Yesu.  Chifukwa uthenga wabwino uluonse umalembedwa kwa anthu osiyanasiyana, 
                    onsewo amayimira mbali zosiyana za moyo wa Khristu. 
 |  
               
                | 1. Yohane anati chani pomaliza pa uthenga wake wabwino? Yohane 
                  21:25 . . .
 
 |  2. Ndi mayina ena ati amene Yesu amatchulidwa 
              mu buku la Mateyu?   a. Mateyu 1:21  b. Mateyu 1:23 c. Mateyu 3:17  d. Mateyu 12:8 e. Mateyu 16:16  f. Mateyu 19:16 3. Kodi Yesu amatchedwa yani mu mabuku limene likuyenderana ndi 
              Bailo?  a. Marko 5:6-7  b. Luka 5:5  c. Yohane 1:35-36  d. John 1:49  e. 1 Akolinto 1:6-7  
               
                | Josephus (Joh-SEE-fus), Wodziwa za mbiri wa chi 
                  Yuda amene anabadwa mu chaka cha A.D. 37 amene anali wosakhulupirira 
                  , analemba zoona za kupachikidwa kwa Yesu. Ngakhale kuti Josephus 
                  samakhulupirira kuti Yesu ndi Mesiya, analemba izi zokhudzana 
                  ndi Yesu:  “Tsopano, panali munthu uyu wa nzeru , ngati nkoyenera 
                    kumutcha munthu, poti anali wochita ntchito za bwino, mpunzitsi 
                    wa anthu wa choonadi. Anakopa Ayuda ngakhale a Mitundu. Anali 
                    Khristu, ndipo pamene Pilato pa kukhumba kwa anthu akuluakulu 
                    mwa ife, analamula apachikidwe pa mtanda, iwo anankonda Iye 
                    poyamba sanantaye; poti anaonekeranso kwa iwo wamoyo pa tsiku 
                    la chitatu, monga momwe aneneri a uzimu analoserandi zikwi 
                    khumi za zinthu zodabwitsa zokhudza Iye. Ndipo mtundu wa Akhristu 
                    wotchedwa chifukwa cha Iye ukanalipo osatha mpaka lero.”  —Antiquities
 |  Ma uneneri ochepa okhudza 
              Mesiya   
               
                | Uneneri  | Kukwaniritsidwa  |   
                | Adzabadwa mwa namwali. | Kubadwa mwa namwali Yesu |   
                | Yesaya 7:14 
                    (742B.C.)Chifukwa chache Ambuye mwini yekha
 adzakupatsani chizindikiro, taonani namwali
 adzaima, nadzabala mwana wa mwamuna,
 nadzamucha dzina lache Imanueli. (NASB)
 
 
 
 | Mateyu 1:22-23 Ndipo zonsezi zinakhala kuti chikachitidwe chonenedwa ndi 
                    Ambuye mwa mneneri, ndi kuti, Onani namwali adzaima, nadzabala 
                    mwana wa mwamuna dzina lace, Emanueli;
 (ndilosandulika, “Mulungu nafe”).
 |   
                | Malo ake obadwira 
 | Kubadwa kwa Yesu mu Betelehem.
 |   
                | Micah 5:2 (710B.C.)Ambuye akuti, “Betelehemu Efrata, ndiwe
 wa ngono kuti ukhale mwa zikwi za Yuda, mwa iwe mudzatuluka 
                    wowereza mu Israyeli;
 matulukiro ake ndiwo a kale lomwe, kuyambira nthawi yosayamba.
 
 | Mateyu 2:1a Yesu adabadwa mu mzinda
 wa Betelehemu wa Yudea mu nthawi imene Herodi adali mfumu.
 |   
                | Adzakanidwa ndi anthu Ache. 
 | Yesu adakanidwa.
 
 |   
                | Isaiah 53:3 (712B.C.)Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu; munthu wa zisoni, 
                    ndiwodziwa zowawa; ndipo ananyozedwa monga munthu ombisira 
                    anthu nkhope zao; ndipo ife sitinamulemekeza.
 | Yohane 1:11 Anadza kwa zache za Iye yekha, koma dziko silidamuzindikira 
                  Iye.
 |   
                | Adzaperekedwa ndi bwenzi | Yesu adaperekedwa ndi m'modzi mwa ophunzira. |   
                | Salimo 41:9 (1062B.C.) Ngakhale bwenzi langa leni leni, amene
 ndamkhulupirira, ndiye amene anadyako mkate wanga, adandikwezera 
                  chidendene chache.
 
 | Marko 14:10 Ndipo Yudase Iskariote, ndiye mmodzi wa khumi ndi awiriwo, anachoka 
                  napita kwa ansembe akulu, kuti akampereke Iye kwa iwo.
 |   
                | Adzauka kwa akufa. | Yesu anauka patatha masiku atatu m'manda. |   
                | Salimo 16:10 (1040 
                  B.C.) …akuti simudzasiya moyo wanga kumanda;
 simudzalora okondedwa wanu avunde.
 
 
 
 | Mateyu 28:5-6Koma ngelo anayankha nati kwa akaziwo,
 "Musaope inu; pakuti ndidziwa inu muli kufuna Yesu, amene 
                    anapachikidwa. Iye mulibe muno iai; pakuti anauka, monga ananena 
                    .idzani muno mudzaone malo omwe anagonamo Ambuye.”
 |  
 
               
                | 4. Ziganizo zili mmusimu zikukamba za mbiri za Yesu. Onani pa 
                  mafunso oti
 muyankhe, ndi zofananiza malemba a chiganizo ndi mau oyenerera 
                  mbaibulo:
 a. Makolo Ake .......................b. Ubatizo Wake .....................c. 
                    Wake choyamba chake
 |  
               
                | “Khristu ndi fanizo la Mulungu wosaonekayo..."
 —Akolose 1:15
 
 |  Pemphero Lotseka Zikomo Ambuye Mulungu. Taphunzira za mbiri za Yesu mu phunziro 
              ili. Tiphunzitseni za mbiri pamene tikupitiliza maphunziro awa. 
              Tithanndizeni kupeza nthawi yowerenga phunziro ya sabata ya mawa. 
              Tapemphera mu dzina la Yesu, ame.   |  |